39 Koma anadzanso 7 Nikodemo, amene anadza kwa iye usiku poyamba paja, alikutenga cisanganizo ca mure ndi aloe, monga miyeso zana.
40 Pamenepo anatenga mtembo wa Yesu, nauzenenga ndi nsaru zabafuta pamodzi ndi zonunkhira, monga mwa maikidwe a maliro a Ayuda.
41 Koma kunali munda kumalo kumene anapacikidwako, ndi m'mundamo munali manda atsopano m'mene sanaikidwamo munthu ali yense nthawi zonse.
42 8 Pomwepo ndipo anaika Yesu, cifukwa ca tsiku lokonzera la Ayuda, pakuti mandawo anali pafupi.