29 nadzaturukira, amene adacita zabwino, kukuuka kwa moyo; koma amene adacita zoipa kukuuka kwa kuweruza.
30 Sindikhoza kucita kanthu kwa Ine ndekha; monga momwe ndimva ndiweruza; ndipo maweruzidwe anga ali olungama; cifukwa kuti sinditsata cifuniro canga, koma cifuniro ca Iye ondituma Ine.
31 Ngati ndicita umboni wa Ine ndekha, umboni wanga suli woona.
32 Wocita umboni wa Ine ndi wina; ndipo ndidziwa kuti umboni umene iye andicitira Ine uli woona.
33 Inu munatuma kwa Yohane, ndipo iye anacitira umboni coonadi.
34 Ndipo Ine sindilandira umboni kwa munthu: koma ndinena izi, kuti inu mukapulumutsidwe.
35 Iyeyo anali nyali yoyaka ndi yowala; ndipo inu munafuna kukondwera m'kuunika kwace kanthawi.