40 ndipo 3 simufuna kudza kwa Ine, kuti mukhale nao moyo.
41 4 Ulemu sindiulandira kwa anthu.
42 Koma ndikudziwani inu, kuti mulibe cikondiea Mulungu mwa inu nokha.
43 Ndadza Ine m'dzina la Atate wanga, ndipo simundilandira Ine; akadza wina m'dzina lace la iye mwini, iyeyu mudzamlandira.
44 Mungathe inu bwanji kukhulupira, 5 popeza mulandira ulemu wina kwa mnzace ndipo ulemu wakucokera kwa Mulungu yekha simuufuna?
45 Musayesa kuti Ine ndidzakunenezani inu kwa Atate; 6 pali wakukunenezani, ndiye Mose, amene inu mumtama.
46 Pakuti mukadakhulupirira Mose, mukadakhulupirira Ine; 7 pakuti iyeyu analembera za Ine.