6 Yesu, pakuona ameneyo alikugona, ndipo anadziwa kuti anatero nthawi yaikuru pamenepo, ananena naye, Ufuna kuciritsidwa kodi?
7 Wodwalayo anayankha, Ambuye, ndiribe wondibvika ine m'thamanda, pali ponse madzi abvundulidwa; koma m'mene ndirinkudza ine, wina atsika ndisanatsike ine.
8 Yesu ananena naye, Tauka, yalula mphasa yako, nuyende,
9 Ndipo pomwepo munthuyu anacira, nayalula mphasa yace, nayenda.Koma tsiku lomwelo linali la Sabata.
10 Cifukwa cace Ayuda ananena kwa wociritsidwayo, Ndi Sabata, ndipo sikuloledwa kwa iwe kuyalula mphasa yako.
11 Koma iyeyu anayankha iwo, iye amene anandiciritsa, yemweyu anati kwa ine, Yalula mphasa yako, nuyende,
12 Anamfunsa, Munthuyo ndani wonena ndi iwe, Yalula mphasa yako, nuyende?