8 Mmodzi wa akuphunzira ace, Andreya, mbale wace wa Simoni Petro, ananena ndi Iye,
9 Pali mnyamata pano, amene ali nayo mikate isanu yabarele, ndi tinsomba tiwiri; koma nanga izi zifikira bwanji ambiri otere?
10 N ati Yesu, Akhalitseni anthu pansi, Ndipo panali udzu wambiri pamalopo, Pamenepo amunawo anakhala pansi, kuwerenga kwao monga zikwi zisanu.
11 Pomwepo Yesu anatenga mikateyo; ndipo pamene adayamika, anagawira iwo akukhala pansi; momwemonso ndi tinsomba, monga momwe iwo anafuna.
12 Ndipo pamene adakhuta, Iyeananena kwa akuphunzira ace, Sonkhanitsani makombo kuti kasatayike kanthu.
13 Pomwepo anasonkhanitsa, nadzaza mitanga khumi ndi iwiri ndi makombo a mikate isanuyo yabarele, amene anatsalira anadyawo.
14 Cifukwa cace, anthu, poona cizindikilo cimene anacita, ananena, kuti, Ameneyo ndiye mneneri ndithu wakudzayom'dziko lapansi.