29 Ndipo wondituma Ine ali ndi Ine; sanandisiya Ine pa ndekha; cifukwa ndicita Ine rimene zimkondweretsa iye nthawi zonse.
30 Pakulankhula iye zimenezi, ambiri anakhulupirira iye.
31 Cifukwa cace Yesu ananena kwa Ayuda aja adakhulupirira iye, Ngati mukhala inu m'mau anga, muli akuphunzira anga ndithu;
32 ndipo mudzazindikira coonadi, ndipo coonadi cidzakumasulani.
33 Anamyankha iye, Tiri mbeu ya Abrahamu, ndipo sitinakhala akapolo a munthu nthawi iri yonse; munena bwanji; Mudzayesedwa aufulu?
34 Yesu anayankha iwo, nati, Indetu, indetu, ndinena kwa inu kuti yense wakucita cimo ali kapolo wa cimolo.
35 Koma kapolo sakhala m'nyumba nthawi yonse; mwana ndiye akhala nthawi yonse.