13 Atamcotsa iye mumseu, anthu onse anapitirira kumsata Yoabu kukalondola Seba mwana wa Bikri.
14 Ndipo anapyola mapfuko onse a Israyeli kufikira ku Abeli ndi ku Betimaaka, ndi kwa Aberi onse; iwo nasonkhana pamodzi namlondolanso.
15 Ndipo anadza nammangira misasa m'Abeli wa Betimaaka, naundira nthumbira pa mudziwo, ndipo unagunda tioga; ndipo anthu onse akukhala ndi Yoabu anakumba lingalo kuti aligwetse.
16 Pamenepo mkazi wanzeru wa m'mudzimo anapfuula, kuti, Imvani, imvani; munene kwa Yoabu, Bwerani pafupi kuno kuti ndgankhule nanu.
17 Ndipo anayandikira kwa mkaziyo; ndi mkaziyo anati, Ndinu Yoabu kodi? iye nayankha, Ndine amene. Pamenepo ananena naye, Imvani mau a mdzakazi wanu. Iye nayankha, Ndirikumva.
18 Ndipo iye analankhula, nati, Kale adafunena kuti, Zoonadi adzapempha uphungu ku Abeli; ndipo potero mrandu udafukutha.
19 Inendine wa awo amene ali amtendere ndi okhulupirika m'Israyeli; inu mulikufuna kuononga mudzi ndi mai wa m'Israyeli; mudzamezerang colowa ca Yehova?