4 Poturuka nalo tsono pamodzi ndi likasa la Mulungu m'nyumba ya Abinadabu iri pacitunda, Ahio anatsogolera likasalo.
5 Ndipo Davide ndi a nyumba yonse ya Israyeli anasewera pamaso pa Yehova, ndi zoyimbira za mitundu mitundu za mlombwa, ndi azeze, ndi zisakasa ndi malingaka, ndi masece, ndi nsanje.
6 Ndipo pofika iwo ku dwale la Nakoni, Uza anatambasula dzanja lace, nacirikiza likasa la Mulungu; cifukwa ng'ombe zikadapulumuka.
7 Pomwepo mkwiyo wa Yehova udayaka pa Uza, ndipo Mulungu anamkantha pomwepo, cifukwa ca kusalingiriraku; nafa iye pomwepo pa likasa la Mulungu.
8 Ndipo kudaipira Davide, cifukwa Yehova anacita cipasulo ndi Uza; nacha-malowo Cipasulo ca Uza, kufikira lero lino.
9 Ndipo Davide anaopa Yehova tsiku lomwelo; nati, Ngati likasa la Yehova lidzafika kwa ine?
10 Momwemo Davide sanafuna kudzitengera likasa la Yehova lidze ku mudzi wa Davide; koma Davide analipambutsira ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.