8 Pamene mumanga nyumba yatsopano, muzimanga kampanda pa tsindwi lace, kuti ungatengere nyumba yanu mwazi, akagwako munthu.
9 Musamabzala mbeu zosiyana m'munda wanu wamphesa, kuti zingaipsidwe mbeu zonse udazibzala, ndi zipatso za munda wamphesa zomwe.
10 Musamalima ndi buru ndi ng'ombe zikoke pamodzi.
11 Musamabvala nsaru yosokonezeka yaubweya pamodzi ndi thonje.
12 Mudzipangire mphonje pa ngondya zinai za copfunda canu cimene mudzipfunda naco.
13 Munthu akatenga mkazi, nalowana naye, namuda,
14 namneneza zoutsa mbiri yamanyazi, ndi kumveketsa dzina loipa, ndi kuti, Ndinamtenga mkazi uyu, koma polowana nave sindinapeza zizindikilo zakuti ndiye namwali ndithu;