13 Naimirire awa pa phiri la Ebala, kutemberera: Rubeni, Gadi, ndi Aseri, ndi Zebuloni, Dani, ndi Nafitali.
14 Ndipo ayankhe Alevi ndi kunena kwa amuna onse a Israyeli, ndi mau omveka.
15 Wotembereredwa munthu wakupanga fano losema kapena loyenga, lonyansidwa nalo Yehova, nchito ya manja a mmisiri, ndi kuliika m'malo a m'tseri. Ndipo anthu onse: ayankhe ndi kuti, Amen.
16 Wotembereredwa iye wakupeputsa atate wace kapena mai wace. Ndi anthu onse anene, Amen.
17 Wotembereredwa iye wakusendeza malire a mnansi wace. Ndi anthu onse anene, Amen.
18 Wotembereredwa wakusokeretsa wakhungu m'njira, Ndi anthu onse anene, Amen.
19 Wotembereredwa iye wakuipsa mlandu wa mlendo, mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye. Ndi anthu onse anene, Amen.