41 Mudzabala ana amuna ndi akazi, osakhala nao, popeza adzalowa ukapolo.
42 Mitengo yanu yonse ndi zipatso za nthaka yanu zidzakhala zao zao za dzombe.
43 Mlendo wokhala pakati panu adzakulira-kulira inu, koma inu mudzacepera-cepera.
44 Iye adzakukongoletsani, osamkongoletsa ndinu; iye adzakhala mutu, koma inu ndinu mcira.
45 Ndipo matemberero awa onse adzakugwerani, nadzakulondolani, ndi kukupezani, kufikira mwaonongeka, popeza simunamvera mau a Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ace ndi malemba ace amene anakulamulirani;
46 ndipo zidzakukhalirani inu ndi mbeu zanu ngati cizindikilo ndi cozizwa, nthawi zonse.
47 Popeza simunatumikira Yehova Mulungu wanu ndi cimwemwe ndi mokondwera mtima, cifukwa ca kucuruka zinthu zonse;