11 Ndi pambuyo pace Eloni Mzebuloni anaweruza Israyeli; naweruza Israyeli zaka khumi.
12 Nafa Eloni Mzebuloni naikidwa m'Aijaloni m'dziko la Zebuloni.
13 Ndi pambuyo pace Abidonf mwana wa Hilele wa ku Piratoni anaweruza Israyeli.
14 Ndipo anali nao ana amuna makumi anai ndi zidzukulu zazimuna makumi atatu, akuyenda okwera pa ana a aburu makumi asanu ndi awiri; naweruza Israyeli zaka zisanu ndi zitatu.
15 Nafa Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni, naikidwa m'Piratoni m'dziko la Efraimu ku mapiri a Amaleki.