1 Ndipo cizindikilo cacikuru cinaoneka m'mwamba; mkazi wobvekedwa dzuwa, ndi mwezi ku mapazi ace, ndi pamutu pace korona wa nyenyezi khumi ndi ziwiri;
2 ndipo anali ndi pakati; ndipo apfuula alimkubala, ndi kumva zowawa zakubala.
3 Ndipo cinaoneka cizindikilo cina m'mwamba, taonani, cinjoka cofiira, cacikuru, cakukhala nayo mitu isanu ndi iwiri, ndi nyanga khumi, ndi pamutu pace nduwira zacifumu zisanu ndi ziwiri.
4 Ndipo mcira wace uguza limodzi la magawo atatu a nyenyezi zam'mwamba, nuziponya padziko. Ndipo cinjoka cinaimirira pamaso pa mkazi akuti abale, kuti, akabala, ico cikalikwire mwana wace.