4 Iwo ndiwo amene sadetsedwa pamodzi ndi akazi; pakuti ali anamwali. Iwo ndiwo amene atsata Mwanawankhosa kulikonse amukako. Iwowa anagulidwa mwa anthu, zipatso zoundukulakwa Mulungu ndi kwa Mwanawankhosa.
5 Ndipo m'kamwa mwao simunapezedwa bodza; ali opanda cirema.
6 Ndipo ndinaona mngelo wina alikuuluka pakati pa mlengalenga, wakukhala nao Uthenga Wabwino wosatha, aulalikire kwa iwo akukhala padziko, ndi kwa mtundu uti wonse ndi pfuko ndi manenedwe ndi anthu j
7 ndi kunena ndi mau akuru, Opani Mulungu, mpatseni ulemerero; pakuti yafika nthawi ya ciweruziro cace; ndipo mlambireni iye amene analenga m'mwamba ndi mtunda ndi nyanja ndi akasupe amadzi,
8 Ndipo anatsata mngelo wina mnzace ndi kunena, Wagwa, wagwa, Babulo waukuru umene unamwetsako mitundu yonse ku vinyo wa mkwiyo wa cigololo cace.
9 Ndipo anawatsata mngelo wina, wacitatu, nanena ndi mau akuru, Ngati wina alambira ciromboco, ndi fane lace, nalandira lembapamphumi pace, kapena pa dzanja lace,
10 iyenso adzamwako kuvinyo wa mkwiyo wa Mulungu, wokonzeka wosasanganiza m'cikho ca mkwiyo wace; ndipo adzazunzika ndi moto ndi sulfure pamaso pa angelo oyera mtima ndi pamaso pa Mwanawankhosa j