1 Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam'munda.
2 Nthambi iri yonse ya mwa Ine yosabala cipatso, aicotsa; ndi iri y'onse yakubala cipatso, aisadza, kuti ikabale cipatso cocuruka.
3 Mwakhala okonzeka tsopano inu cifukwa ca mau amene ndalankhula ndi inu,
4 Khalani mwa Ine, ndi Ine mwa inu. Monga nthambi siingathe kubala cipatso pa yokha, ngati siikhala mwampesa; motere mulibe inunso ngati simukhala mwa Ine.