7 ndi mlezo, umene unali pamutu pace, wosakhala pamodzi ndi nsaru zabafuta, koma wopindika padera pamalo pena.
8 Pamenepo tsono analowanso wophunzira winayo, amene anayamba kufika kumanda, ndipo anaona, nakhulupira.
9 Pakuti kufikira pomwepo sanadziwa lembo lakuti ayenera iye kuuka kwa akufa.
10 Cifukwa cace akuphunzirawo anacokanso, kunka kwao.
11 Koma Mariya analikuima kumanda kunja, alikulira. Ndipo m'mene alikulira anawerama cisuzumirire kumanda;
12 ndipo anaona angelo awiri atabvala zoyera, alikukhala mmodzi kumutu, ndi wina kumiyendo, kumene mtembo wa Yesu udagona.
13 Ndipo iwowa ananena kwa iye, Mkazi, uliranji? Ananena nao, Cifukwa anacotsa Ambuye wanga, ndipo sindidziwa kumene anamuika iye.