17 Ndipo Omri anacoka ku Gibetoni, ndi Aisrayeli onse naye, nakamangira misasa Tiriza.
18 Kunali tsono, pakuona Zimri kuti nkhondo yalowa m'mudzi, anakwera pa nsanja ya nyumba ya mfumu, nadzitenthera ndi mota nyumba ya mfumu, nafa;
19 cifukwa ca macimo ace anacimwawo, pakucita coipa pamaso pa Yehova; popeza anayenda m'njira ya Yerobiamu, ndi m'chimo lace anacimwa nalolo, nacimwitsa nalo Aisrayeli.
20 Macitidwe ena tsono a Zimri, ndi ciwembu anacicitaco, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?
21 Pamenepo anthu a Israyeli anagawika pakati, anthu ena anatsata Tibini mwana wa Ginati kumlonga ufumu, ena natsata Omri.
22 Koma anthu akutsata Omri anapambana iwo akutsata Tibini mwana wa Ginati; nafa Tibini, Omri nakhala mfumu.
23 Caka ca makumi atatu ndi cimodzi ca Asa mfumu ya Yuda, Omri anayamba kukhala mfumu ya Israyeli, nakhala zaka khumi ndi ziwiri; ku Tiriza anali mfumu zaka zisanu ndi cimodzi.