14 Nati iye, Ndacitira cangu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israyeli ataya cipangano canu, nagumula maguwa a nsembe anu, napha aneneri anu ndi lupanga; ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuucotsa.
15 Ndipo Yehova anati kwa iye, Bwerera ulendo wako, udzere kucipululu kumka ku Damasiko, ndipo utafikako udzoze Hazaeli akhale mfumu ya Aramu;
16 ukadzozenso Yehu mwana wa Nimsi akhale mfumu ya Israyeli; ukadzozenso Elisa mwana wa Safati wa ku Abelimehola akhale mneneri m'malo mwako.
17 Ndipo kudzacitika Yehu adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Hazaeli; ndi Elisa adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Yehu,
18 Ndiponso ndidasiya m'lsrayeli anthu zikwi zisanu ndi ziwiri osagwadira Baala maondo ao, osampso-mpsona ndi milomo yao.
19 Tsono anacokako, napeza Elisa mwana wa Safati alikukoketsa cikhasu ng'ombe ziwiri ziwiri magori khumi ndi awiri, iye yekha anakhala pa gori lakhumi ndi ciwiri; ndipo Eliya anamka kunali iyeyo, naponya copfunda cace pa iye.
20 Ndipo iye anasiya ng'ombe zija, namthamangira Eliya, nati, Ndiloleni ndithange ndakapsompsona atate wanga ndi amai wanga; nditatero ndidzakutsatani. Nati iye, Bwerera, ndakucitanji?