13 Ndikadacita conyenga pa moyo wace, palibe mrandu ubisika kwa mfumu; ndipo inu nomwe mukadanditsuta.
14 Pomwepo Yoabu anati, Sindiyenera kucedwa nawe. Natenga mikondo itatu nagwaza nayo mtima wa Abisalomu alikukhala wamoyo pakati pa mtengowo.
15 Ndipo anyamata khumi onyamula zida zace za Yoabu anamzungulira Abisalomu namkantha namupha.
16 Ndipo Yoabu analiza lipenga, ndipo anthu anabwerera naleka kupitikitsa Aisrayeli; pakuti Yoahu analetsa anthuwo.
17 Ndipo anatenga Abisalomu namponya m'cidzenje cacikuru kunkhalangoko; naunjika pamwamba pace mulu waukuru ndithu wamiyala; ndipo Aisrayeli onse anathawa yense ku hema wace.
18 Koma Abisalomu akali moyo adatenga nadziutsira coimiritsaco ciri m'cigwa ca mfumu; pakuti anati, Ndiribe mwana wamwamuna adzakhala cikumbutso ca dzina langa; nacha coimiritsaco ndi dzina la iye yekha; ndipo cichedwa cikumbutso ca Abisalomu, kufikira lero lomwe.
19 Pomwepo Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, Ndithamange nditengere mfumu mau kuti Yehova wabwezera cilango adani ace.