15 ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi monga mwa mtundu wace;
16 ndi nkhutukutu, ndi mancici, ndi tsekwe;
17 ndi bvuwo, ndi dembu, ndi nswankhono;
18 ndi iodwa, ndi cimeza, monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.
19 Ndipo zokwawa zonse zakuuluka muziyesa zonyansa; musamazidya.
20 Mbalame zonse zosadetsa muyenera kumadya.
21 Musamadya cinthu ciri conse citafa cokha; muzipereka ico kwa mlendo ali m'mudzi mwanu, acidye ndiye; kapena ucigulitse kwa mlendo; popeza ndinu mtundu wa anthu wopatulika wa Yehova Mulungu wanu. Musamaphika mwana wa mbuzi mu mkaka wa mace.