1 Pamenepo tinabwerera, ndi kuyenda kumka kucipululu, kutsata njira ya Nyanja Yofiira, monga Yehova adanena ndi ine; ndipo tinapaza phiri la Seiri masiku ambiri.
2 Ndipo Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,
3 Yakwanira nthawi yakupaza inu phiri ili; tembenukani kumka kumpoto,
4 Ndipo uuze anthu, ndi kuti, Mukapite kubzyola malire a abale anu, ana a Bsau okhala m'Seiri; ndipo adzakuopani; mucenjere ndithu;