13 Ukani tsopano, olokani mtsinje wa Zeredi. Ndipo tinaoloka mtsinje wa Zeredi.
14 Ndipo masiku amene tinayenda kucokera ku Kadesi Barinea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m'cigono, monga Yehova adawalumbirira.
15 Komanso dzanja la Yehova linatsutsana nao, kuwaononga m'cigono, kufikira adawatha.
16 Ndipo kunali, atatha kufa amuna onse ankhondo mwa anthu,
17 Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,
18 Lero lomwe utumphe malire a Moabu, ndiwo Ari.
19 Ndipo pamene uyandikiza popenyana ndi ana a Amoni, usawabvuta, kapena kuutsana nao; popeza sindidzakupatsako dziko la ana a Amoni likhale lako lako; popeza ndinapatsa ana a Loti ili likhale lao lao.