1 Akapeza munthu waphedwa m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu lanu, nagona pamunda, wosadziwika wakumkantha,
2 pamenepo azituruka akuru anu ndi oweruza anu, nayese ku midzi yomzinga wophedwayo;
3 ndipo kudzali kuti mudzi wakukhala kufupi kwa munthu wophedwayo, inde akuru a mudzi uwu atenge ng'ombe yamsoti yosagwira nchito, yosakoka goli;
4 ndipo akuru a mudzi uwu atsike nao msotiwo ku cigwa coyendako madzi, cosalima ndi cosabzala, naudula khosi msotiwo m'cigwamo;
5 ndipo ansembe, ana a Levi, ayandikize; pakuti Yehova Mulungu wanu anasankha iwo kumtumikira ndi kudalitsa m'dzina la Yehova; ndipo kutengana konse ndi kupandana konse kukonzeke monga mwa mau awa.
6 Ndipo akuru onse a mudziwo wokhala pafupi pa munthu wophedwayo azisamba manja ao pa msoti woudula khosi m'cigwamo;
7 nayankhe nati, Manja athu sanakhetsa mwazi uwu, ndi maso athu sanauona.