1 Munthu wophwetekwa, wophwanyika kapena wofulika, asalowe m'msonkhano wa Yehova.
2 Mwana wa m'cigololo asalowe m'msonkhano wa Yehova, ngakhale mbadwo wace wakhumi usalowe m'msonkhano wa Yehova.
3 M-amoni kapena Mmoabu asalowe m'msonkhano wa Yehova; ngakhale mbadwo wao wakhumi usalowe m'msonkhano wa Yehova, ku nthawi zonse;
4 popeza sanakukumikani ndi mkate ndi madzi m'njira muja munaturuka m'Aigupto; popezanso anakulembererani Balamu mwana wa Beori wa ku Petori wa Mesapotamiya, kuti akutemberereni.