8 Ana obadwa nao a mbadwo wacitatu alowe m'msonkhano wa Yehova.
9 Nkhondo yanu ikaturuka pa adani anu, mudzisunge kusacita coipa ciri conse.
10 Pakakhala munthu pakati pa inu, ndiye wosayera cifukwa cocitika usiku, azituruka kunja kwa cigono, asalowe pakati pa cigono;
11 koma kudzali pofika madzulo, asambe m'madzi; ndipo litalowa dzuwa alowe pakati pa cigono.
12 Mukhale nao malo kunja kwa cigono kumene muzimukako kuthengo;
13 nimukhale naco cokumbira mwa zida zanu; ndipo kudzali, pakukhala inu pansi kuthengo mukumbe naco, ndi kutembenuka ndi kufotsera cakuturukaco;
14 popeza Yehova Mulungu wanu ayenda pakati pa cigono canu, kukupulumutsani ndi kupereka adani anu pamaso panu; cifukwa cace cigono canu cikhale copatulika; kuti angaone kanthu kodetsa mwa inu, ndi kukupotolokerani.