6 pamenepo anati kwa iye, Unene tsono Shiboleti; ndipo akati, Siboleti, osakhoza kuchula bwino, amgwira namupha padooko pomwe pa Yordano; ndipo anagwa a Efraimu nthawi ija, zikwi makumi anai mphambu ziwiri.
7 Ndipo Yefita anaweruza Israyeli zaka zisanu ndi cimodzi; nafa Yefita Mgileadi, naikidwa m'mudzi wina wa Gileadi.
8 Ndi pambuyo pace Ibzani wa ku Betelehemu anaweruza Israyeli.
9 Ndipo anali nao ana amuna makumi atatu; ndi ana akazi makumi atatu anawakwatitsa kwina, natengera ana ace amuna ana akazi makumi atatu ocokera kwina. Ndipo anaweruza Israyeli zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Nafa Ibzani naikidwa ku Betelehemu.
11 Ndi pambuyo pace Eloni Mzebuloni anaweruza Israyeli; naweruza Israyeli zaka khumi.
12 Nafa Eloni Mzebuloni naikidwa m'Aijaloni m'dziko la Zebuloni.