22 Nati Manowa kwa mkazi wace, Tidzafa ndithu pakuti taona Mulungu.
23 Koma mkazi wace ananena naye, Yehova akadafuna kutipha, sakadalandira nsembe yopsereza ndi nsembe yaufa pa dzanja lathu, kapena kutionetsa izi zonse, kapena kutimvetsa zoterezi nthawi yino.
24 Ndipo mkaziyo anabala mwana wamwamuna namucha dzina lace Samsoni; nakula mwanayo, Yehova namdalitsa.
25 Ndipo mzimu wa Yehova unayamba kumfulumiza mtima ku misasa ya Dani pakati pa Zora ndi Esitaoli.