32 Cifukwa cace anamucha tsiku lija Yerubaala, ndi kuti, Amnenece mlandu Baala popeza anamgamulira guwa lace la nsembe.
33 Pamenepo Amidyani onse ndi Aamaleki ndi ana a kum'mawa anasonkhana pamodzi naoloka, namanga misasa m'cigwa ca Yezreeli.
34 Koma mzimu wa Yehova unabvana Gideoni; naomba lipenga iye, ndi a banja la Abieziri analalikidwa kumtsata iye.
35 Ndipo anatuma mithenga kwa Manase konse; ndi iwonso analalikidwa kumtsata iye; natuma mithenga kwa Aseri, ndi kwa Zebuloni, ndi kwa Nafitali; iwo nadzakomana nao.
36 Ndipo Gideoni anati kwa Mulungu, Mukadzapulumutsa Israyeli ndi dzanjalanga monga mwanena,
37 taonani, ndidzaika cikopa ca ubweya popunthira tirigu; pakakhala mame pacikopa pokha, ndi panthaka ponse pouma, pamenepo ndidzadziwa kuti mudzapulumutsa Israyeli ndi dzanja langa monga mwanena.
38 Ndipo kunatero; pakuti anauka mamawa, nafinya cikopaco, nakamula mame a pacikopa, madzi ace odzala mbale.