13 Koma ana a Israyeli sanainga Agesuri kapena Amaakati; koma Gesuri, ndi Maakati amakhala pakati pa Israyeli, mpaka lero lino.
14 Koma pfuko la Levi sanalipatsa colowa; nsembe za Yehova Mulungu wa Israyeli, zocitika ndi moto, ndizo colowa cace, monga iye adanena naye.
15 Ndipo Mose anapatsira pfuko la ana a Rubeni monga mwa mabanja ao.
16 Malire ao anayambira ku Aroeri wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uli pakati pa cigwa ndi cidikha conse ca ku Medeba;
17 Hesiboni ndi midzi yace yonse yokhala pacidikha; Diboni, ndi Bamoto-baala ndi Betibaala-Meoni;
18 ndi Yahaza ndi Kedemotu, ndi Mefaata;
19 ndi Kinyataimu, ndi Sibima, ndi Zeretisahara, m'phiri la kucigwa;