Yoswa 2 BL92

Yoswa atuma anthu awiri azonde Yeriko

1 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, ali ku Sitimu, anatuma amuna awiri mosadziwika kukazonda, ndi kuti, Mukani, mulipenye dzikolo, ndi ku Yeriko. Ndipo anamuka nalowa m'nyumba ya mkazi wadama, dzina lace Rahabi, nagona momwemo.

2 Ndipo wina anaiuza mfumu ya Yeriko, kuti, Taonani, usiku uno alowa muno amuna a ana a Israyeli, kulizonda dziko.

3 Ndipo mfumu ya Yeriko inatuma wina kwa Rahabi, ndi kuti, Turutsa amunawo anafika kwanu, amene analowa m'nyumba mwako; popeza anadzera kulizonda dziko lonse.

4 Koma mkaziyo anatenga amuna awiriwo, nawabisa; natero, Inde, amunawo anandifikira; koma sindinadziwa uko afuma;

5 ndipo m'mene akadati atseke pacipata, kutada, anaturuka amunawo; uko anamuka amunawo osakudziwa ine; muwalondole msanga, pakuti mudzawapeza.

6 Koma adawakweretsa patsindwi, nawabisa ndi mitengo yanthamza yoyanika patsindwi.

7 Ndipo amunawo anawalondola pa njira ya ku Yordano yomka kudooko; ndipo ataturuka akuwalondola, anatseka pacipata.

8 Koma asanagone iwo, anawakwerera patsindwi iye,

9 nati kwa amunawo, Ndidziwa kuti Yehova wakupatsani dzikoli, ndi kuti kuopsa kwanu kwatigwera, ndi kuti okhala m'dziko onse asungunuka pamaso panu.

10 Popeza tidamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a m'Nyanja Yofiira pamaso panu, muja mudaruruka m'Aigupto; ndi cija munacitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya la Yordano, ndiwo Sihoni ndi Ogi, amene mudawaononga konse.

11 Ndipo titamva ici mitima yathu inasungunuka; anahbenso mtima ndi mmodzi yense, cifukwa ca inu; pakuti Yehova Mulungu wanu, ndiye Mulungu wa m'mwamba umo, ndi pa dziko lapansi.

12 Ndipo tsopano, mundilumbiriretu kwa Yehova, popeza ndakucitirani cifundo, kuti inunso mudzacitira cifundo a m'nyumba ya atate wanga ndi kundipatsa cizindikilo coona,

13 kuti mudzawasunga ndi moyo atate wanga ndi mai wanga, ndi alongo anga ndi abale anga, ndi zonse ali nazo, ndi kupulumutsa miyoyo yathu kuimfa.

14 Ndipo amunawo anati kwa iye, Moyo wathu ndiwo moyo wanu, mukapanda kuulula codzera ife; ndipo kudzakhala kuti, pakutipatsa ife dziko ili Yehova, tidzakucitira cifundo ndi coonadi.

15 Pamenepo anawatsitsa pazenera ndi cingwe; popeza nyumba yace lnali pa linga La mudzi, nakhala iye palingapo.

16 Ndipo anati kwa iwo, Mukani kuphiri, olondola angakupezeni; mubisale kumeneko masiku atatu, mpaka atabwerera olondolawo, pamenepo muyende ulendo wanu.

17 Ndipo amunawo anati kwa iye, Sitidzacimwira lumbiro lako ili watilumbiritsali.

18 Taona, tikadzalowa m'dzikomo ife, uzimanga cingwe ici cofiira pazenera pamene watitsitsira; ndipo udzasonkhanitsa m'nyumbamo atate wako ndi mai wako nui abale ako ndi a m'nyumba onse a atate wako.

19 Ndipo kudzakhala kuti ali yense akadzaturuka pa khomo la nyumba yako kubwalo, imfa imeneyi ndi yace, tiribe kuparamula ife; koma ali yense adzakhala ndi iwe m'nyumba, likamfikira dzanja, imfa imeneyi ndi yathu.

20 Koma ukaulula codzera ifeco tidzamasukira lumbiro lako watilumbiritsali.

21 Nati iye, Momwemo, monga mwa mau anu. Ndipo anawauza amuke, iwo namuka; namanga iye cingwe cofiiraco pazenera.

22 Ndipo anayenda iwo, nafika kuphiri, nakhalako masiku atatu mpaka atabwerera olondolawo; popeza olondolawo anawafunafuna panjira ponse, osawapeza.

23 Pamenepo amuna awiriwo anabwerera, natsika m'phirimo naoloka, nafika kwa Yoswa mwana wa Nuni, namfotokozera zonse zidawagwera.

24 Ndipo anati kwa Yoswa, Zoonadi, Yehova wapereka dziko lonse m'manja mwathu; ndiponso nzika zonse zasungunuka pamaso pathu.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24