Yoswa 15 BL92

Malire a Yuda

1 Ndipo gawo la pfuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao linafikira malire a Edomu, ku cipululu ca Zini kumwera, ku malekezero a kumwera.

2 Ndi malire ao a kumwera, anayambira ku malekezero a Nyanja ya Mcere, ku nyondo yoloza kumwera;

3 naturuka kumwela kwa cikweza ca Akarabi, napitirira ku Zini, nakwera kumwera kwa Kadesi-Barinea, napitirira ku Hezironi, nakwera ku Adara, nazungulira ku Karika;

4 napitirira ku Azimoni, naturuka ku mtsinje wa Aigupto; ndi malekezero a malirewa anali ku Nyanja Yaikuru; awa ndi malire anu a kumwera.

5 Ndi malire a kum'mawa ndiwo Nyanja ya Mcere, mpaka mathiriro ace a Yordano. Ndi malire a kumpoto anayambira nyondo ya nyanja ku mathiriro a Yordano;

6 nakwera malire kumka ku Beti-hogila, napitirira kumpoto kwa Beti-araba; nakwera malire kumka ku mwala wa Bohani mwana wa Rubeni;

7 nakwera malire kumka ku Dibiri, kucokera ku cigwa ca Akori, ndi kumpoto kupenyera Giligala ndiko kundunji kwa cikweza ca Adumi, ndiko kumwela kwa mtsinje; napitirira malire kumka ku madzi a Enisemesi, ndi maturukiro ace anali ku Eni-rogeli;

8 nakwera malire kumka ku cigwa ca mwana wa Hinomu, kumbali kwa Ayebusi, kumwela, ndiko Yerusalemu; nakwera malire kumka kumwamba kwa phiri lokhala patsogolo pa cigwa ca Hinomu kumadzulo, ndilo ku mathero ace a cigwa ca Refai kumpoto,

9 Ndipo analemba malire kuyambira pamwamba pa phiri mpaka citsime ca madzi ca Nefitoa, naturukira malire ku midzi ya phiri la Efroni; ndipo analemba malire kumka ku Baala, ndiwo Kiriyati-Yearimu.

10 Ndipo malire anazungulira kuyambira ku Baala kumka kumadzulo, ku phiri la Seiri, napitirira kumbali kwa phiri la Yearimu kumpoto, ndilo Kesaloni, natsikira ku Beti-semesi, napitirira ku Timina;

11 naturuka malire kumka ku mbali ya Ekroni kumpoto; ndipo analemba malire kumka ku Sikeroni, napitirira ku phiri la Baala, naturuka ku Yabindi; ndipo maturukiro a malire anali kunyanja.

12 Ndi malire a kumadzulo anali ku Nyanja Yaikuru ndiwo malire ace. Awa ndi malire a ana a Yuda pozungulira monga mwa mabanja ao.

13 Koma Yoswa anampatsa Kalebe mwana wa Yefune gawo mwa ana a Yuda, monga Yehova adamlamulira, ndiwo mudzi wa Ariba, ndiye atate wa Anaki, ndiwo Hebroni.

14 Ndipo Kalebe anaingitsako ana amuna atatu a Anaki, ndiwo Sesai, ndi Ahimani, ndi Talimai, ana a Anaki.

15 Nakwera komweko kumka kwa nzika za Dibiri; koma kale dzina la Dibiri ndilo Kiriyati-Seferi.

16 Ndipo Kalebe anati, iye amene akantha Kiriyati-Seferi, naulanda, yemweyo ndidzampatsa Akisa mwana wanga akhale mkazi wace.

17 Ndipo Otiniyeli mwana wa Kenazi, mbale wace wa Kalebe, anaulanda; ndipo anampatsa Akisa mwana wace akhale mkazi wace.

18 Ndipo kunali, m'mene anamdzera, anamkangamiza mwamuna wace kuti apemphe atate wace ampatse munda; ndipo anatsika pa buru; pamenepo Kalebe ananena naye, Ufunanji?

19 Nati iye, Mundipatse dalitso; popeza mwandipatsa dziko la kumwela, ndipatseninso zitsime za madzi. Pamenepo anampatsa zitsime za kumtunda, ndi zitsime za kunsi.

20 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao.

21 Ndipo midzi ya ku malekezero a pfuko la ana a Yuda ku malire a Edomu, kumwela ndiwo, Kabizeeli ndi Ederi, ndi Yaguri;

22 ndi Kina ndi Dimona, ndi Adada;

23 ndi Kedesi, ndi Hazori, ndi ltinani;

24 Zifi ndi Telemu ndi Bealoti;

25 ndi Hazorihadata, ndi Kerioti-hezirondi, ndiwo Hazori;

26 Amamu ndi Sema ndi Moloda;

27 ndi Hazara-gada, ndi Hesimoni, ndi Beti-peleti;

28 ndi Hazara-suala, ndi Beereseba, ndi Bizioti;

29 Baala, ndi lyimu, ndi Ezemu;

30 ndi Elitoladi, ndi Kesili ndi Horima;

31 ndi Zikilaga, ndi Madimana ndi Sanasana;

32 ndi Lebaoti, ndi Siliimu, ndi Aini ndi Rimoni; midzi yonse ndiyo makumi awiri kudza isanu ndi inai; pamodzi ndi miraga yao.

33 Ku cigwa, Esitaoli, ndi Zora ndi Asina;

34 ndi Zoona, ndi Eniganimu, Tapua, ndi Enamu;

35 Yarimutu, ndi Adulamu, Soko, ndi Azeka;

36 ndi Saaraimu, ndi Aditaimu, ndi Gedera, ndi Gederotaimu; midzi khumi ndi inai pamodzi ndi miraga yao.

37 Zenani, ndi Hadasa, ndi Migidala-gadi;

38 ndi Dilani, ndi Mizipe, ndi Yokiteeli;

39 Lakisi ndi Bozikatu ndi Egiloni;

40 ndi Kaboni, ndi Lamasi, ndi, Kitilisi;

41 ndi Gaderotu, Beti-dagoni, ndi Naama, ndi Makeda; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

42 Libina ndi Eteri ndi Asana;

43 ndi Ifita ndi Asina ndi Nezibi;

44 ndi Kehila ndi Akisibu, ndi Maresa; midzi isanu ndi inai pamodzi ndi miraga yao.

45 Ekroni pamodzi ndi midzi yace ndi miraga yao;

46 kuyambira ku Ekroni mpaka kunyanja, yonse ya ku mbali ya Asidodo, pamodzi ndi miraga yao.

47 Asidodo, midzi yace ndi miraga yace; Gaza, midzi yace ndi miraga yace; mpaka mtsinje wa Aigupto, ndi nyanja yaikuru ndi malire ace.

48 Ndi kumapiri Samiri, ndi Yatiri, om Soko;

49 ndi Dana, ndi Kiriyatisana, ndiwo Dibiri;

50 ndi Anabi, ndi Esitemo, ndi Animu;

51 ndi Goseni, ndi Holoni, ndi Gilo; midzi khumi ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

52 Arabu, ndi Duma, ndi Esana;

53 ndi Yanimu, ndi Beti-tapua, ndi Apeka;

54 ndi Humita, ndi Kiriyatiariba, ndiwo Hebroni, ndi Ziori; midzi isanu ndi inai pamodzi ndi miraga yao.

55 Maoni, Karimeli, ndi Zifu, ndi Yuta;

56 ndi Yesireeli, ndi Yokideamu, ndi Zoona;

57 Kaini, Gibea ndi Timina; midzi khumi pamodzi ndi miraga yao.

58 Haluli, Beti-zuru, ndi Gedori,

59 ndi Maaratu, ndi Bete-anotu, ndi Elitekoni; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

60 Kiriyata-Baala, ndiwo KiriyatiYearimu ndi Raba; midzi iwiri pamodzi ndi miraga yao.

61 M'cipululu, Beti-araba, Midini, ndi Sekaka;

62 ndi Nibisani, ndi Mudzi wa Mcere, ndi En-gedi; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

63 Koma ana a Yuda sanakhoza kuingitsa Ayebusi, nzika za Yerusalemu: m'mwemo Ayebusi anakhala pamodzi ndi ana a Yuda, ku Yerusalemu, mpaka lero lino.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24