Yoswa 19 BL92

Malire a Simeoni

1 Ndipo maere aciwiri anamturukira Simeoni, pfuko la ana a Simeoni monga mwa mabanja ao; ndi colowa cao cinali pakati pa colowa ca ana a Yuda.

2 Ndipo anali naco colowa cao Beeri-seba, kapena Seba, ndi Molada;

3 ndi Hazarasuala, ndi Bala, ndi Ezemu;

4 ndi Elitoladi, ndi Betuli, ndi Horimu;

5 ndi Zikilaga, ndi Beti-malikabotu, ndi Hazari-susa:

6 ndi Beti-lebaotu, ndi Saruheni; midzi khumi ndi itatu ndi miraga yao;

7 Aini, Rimoni ndi Eteri ndi Asana; midzi inai ndi miraga yao;

8 ndi miraga yonse yozungulira midzi iyi mpaka Baalata-beeri ndiwo Rama kumwera. Ndico colowa ca pfuko la ana a Simeoni, monga mwa mabanja ao.

9 M'gawo la ana a Yuda muli colowa ca ana a Simeoni; popeza gawo la ana a Yuda linawacurukira; cifukwa cace ana a Simeoni anali naco colowa pakati pa colowa coo.

Malire a Zebuloni

10 Ndipo maere acitatu anakwecera ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao; ndi malire a colowa cao anafikira ku Saridi;

11 nakwera malire ao kumka kumadzulo ndi ku Marala nafikira ku Dabeseti, nafikira ku mtsinje wa patsogolo pa Yokineamu;

12 ndi kucokera ku Saridi anazungulira kumka kum'mawa kumaturukira dzuwa, mpaka malire a Kisilotu-tabori; naturuka kumka ku Daberati, nakwera ku Yafia;

13 ndi pocoka pamenepo anapitirira kumka kum'mawa ku Gati-heferi, ku Etikazini; naturuka ku Remoni umene ulembedwa mpaka ku Nea,

14 nauzungulira malire kumpoto, kumka ku Hanatoni; ndi maturukiro ace anali ku cigwa ca Ifita-eli;

15 ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.

16 Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

Malire a Isakara

17 Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.

18 Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;

19 ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;

20 ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;

21 ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;

22 ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi maturukiro a malire ao anali ku Yordano; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi miraga yao.

23 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Isakara, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.

Malire a Aseri

24 Ndipo maece acisanu analiturukira pfuko la ana a Aseri monga mwa mabanja ao.

25 Ndi malire ao ndiwo Helikati, ndi Hali, ndi Beteni ndi Akisafu;

26 ndi Alameleki, ndi Amadi, ndi Misali; nafikira ku Karimeli kumadzulo ndi ku Sihorilibinati;

27 nazungulira koturukira dzuwa ku Beti-dagoni, nafikira ku Zebuloni ndi ku cigwa ca Ifita-eli, kumpoto ku Beti-emeki, ndi Nehieli; naturukira ku Kabulu kulamanzere,

28 ndi Ebroni, ndi Rehobo, ndi Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni wamkuru;

29 nazungulira malice kumka ku Rama, ndi ku mudzi wa linga la Turo; nazungulira malire kumka ku Hosa; ndi maturukiro ace anali kunyanja, kucokera ku Hebeli mpaka ku Akizibu;

30 Uma womwe ndi Afeki, ndi Rehobo; midzi makumi awiri mphambu iwiri ndi miraga yao,

31 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Aseri monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miragayao.

Malire a Nafitali

32 Maere acisanu ndi cimodzi anaturukira ana a Nafitali, ana a Nafitali monga mwa mabanja ao.

33 Ndipo malire ao anayambira ku Helefi, ku thundu wa ku Zaanani, ndi Adaminekebi, ndi Yabineeli, mpaka ku Lakumu; ndi maturukiro ace anali ku Yordano;

34 nazungulira malire kumka kumadzulo ku Azinotu-tabori, naturukira komweko kumka ku Hukoku; nafikira ku Zebuloni kumwera, nafikira ku Aseri kumadzulo, ndi ku Yuda pa Yordano kum'mawa.

35 Ndipo midzi yamalinga ndiyo Zidimu, Zeri, ndi Hamati, Rakati, ndi Kinereti;

36 ndi Adama, ndi Rama, ndi Hazori;

37 ndi Kedesi, ndi Edrei, ndi Eni-hazori;

38 ndi Ironi, ndi Migidala-eli, Horemu, ndi Betianati, ndi Beti-semesi; midzi khumi ndi isanu ndi inai, ndi miraga yao.

39 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Nafitali, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.

Malire a Dani

40 Maere acisanu ndi ciwiri anaturukira pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao.

41 Ndipo malire a colowa cao anali Zora, ndi Esitaoli ndi Iri-semesi;

42 Saalabini, ndi Aijaloni ndi ltila;

43 ndi Eloni ndi Timna ndi Ekroni;

44 ndi Eliteke, ndi Gibetoni, ndi Baalati;

45 ndi Yehudi, ndi Bene-beraki, ndi Gatirimoni;

46 ndi Me-jarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pajapo.

47 Koma malire a ana a Dani anaturuka kupitirira iwowa; pakuti ana a Dani anakwera nathira nkhondo ku Lesemu, naulanda naukantha ndi lupanga lakuthwa, naulandira, nakhala m'mwemo, naucha Lesemu, Dani; ndilo dzina la Dani atate wao.

48 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

Colowa ca Yoswa

49 Ndipo atatha kuligawa dziko likhale colowa cao monga mwa malire ace, ana a Israyeli anapatsa Yoswa mwana wa Nuni colowa pakati pao;

50 monga mwa lamulo la Yehova anampatsa mudzi umene anawapempha, ndiwo Timinatisera, ku mapiri a Efraimu; ndipo anamangamudziwonakhala m'mwemo.

51 Izi ndizo zolowa anazigawa Eleazare wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akulu a nyumba za atate a mapfuko a ana a Israyeli, zikhale zao zao, ndi kulota maere ku Silo pamaso pa Yehova ku khomo la cihema cokomanako. Momwemo anatha kuligawa dziko.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24