15 Ndipo Mose anapatsira pfuko la ana a Rubeni monga mwa mabanja ao.
16 Malire ao anayambira ku Aroeri wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uli pakati pa cigwa ndi cidikha conse ca ku Medeba;
17 Hesiboni ndi midzi yace yonse yokhala pacidikha; Diboni, ndi Bamoto-baala ndi Betibaala-Meoni;
18 ndi Yahaza ndi Kedemotu, ndi Mefaata;
19 ndi Kinyataimu, ndi Sibima, ndi Zeretisahara, m'phiri la kucigwa;
20 ndi Beti-peori, ndi matsikiro a Pisiga, ndi Beti-yesimotu;
21 ndi midzi yonse ya kucidikha, ndi ufumu wonse wa Sihoni mfumu ya Aamori, wocita ufumu m'Hesiboni, amene Mose anamkantha pamodzi ndi akalonga a Midyani, Evi, ndi Rekemu, ndi Zuri, ndi Huri ndi Reba, akalonga a Sihoni, nzika za m'dziko.