22 ndi Kibizaimu ndi mabusa ace, Betihoroni ndi mabusa ace; midzi inai.
23 Ndipo motapira m'pfuko La Dani, Eliteke ndi mabusa ace, Gibetoni ndi mabusa ace;
24 Aijaloni ndi mabusa ace, Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi inai.
25 Ndipo motapira pa pfukola Manaselogawika pakati, Taanaki ndi mabusa ace, ndi Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi iwiri.
26 Midzi yonse ya mabanja a ana otsala a Kohati ndiyo khumi ndi mabusa ao.
27 Ndipo anapatsa ana a Gerisoni, a mabanja a Alevi, motapira pa pfuko la Manase logawika pakati, Golani m'Basana ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo; ndi Beesitera ndi mabusa ace; midzi iwiri.
28 Ndipo motapira pa pfuko la Isakara, Kisioni ndi mabusa ace, Daberati ndi mabusa ace;