25 Ndipo onse amene adagwa tsiku lija, amuna ndi akazi, ndiwo zikwi khumi ndi ziwiri, anthu onse a ku Ai.
26 Popeza Yoswa sanabweza dzanja lace limene anatambasula nalo nthungo, mpaka ataononga konse nzika zonse za ku Ai.
27 Koma ng'ombe ndi zofunkha za mudzi uwu Israyeli anadzifunkhira monga mwa mau a Yehova amene analamulira Yoswa.
28 Ndipo Yoswa anatentha Ai, nausandutsa muunda ku nthawi yonse, bwinja kufikira lero lino.
29 Ndipo mfumu ya ku Ai, anampacika pamtengo mpaka madzulo; koma polowa dzuwa Yoswa analamulira kuti atsitse mtembo wace pamtengo; ndipo anauponya polowera pa cipata ca mudzi; nauniikako mulu waukuru wamiyala, mpaka lero lino.
30 Pomwepo Yoswa anamangira Yehova Mulungu wa Israyeli guwa la nsembe m'phiri la Ebala,
31 monga Mose mtumiki wa Mulungu adalamulira ana a Israyeli, monga mulembedwa m'buku la cilamulo ca Mose, guwa la nsembe la miyala yosasema, yoti palibe munthu anakwezapo citsulo; ndipo anafukizirapo Yehova nsembe zopsereza, naphera nsembe zoyamika.