1 Ndipo atapita masiku ambiri, mau a Yehova anafika kwa Eliya caka cacitatu, nati, Kadzionetse kwa Ahabu, ndipo ndidzatumiza mvula padziko.
2 Ndipo Eliya anamka kukadzionetsa kwa Ahabu. Ndipo njala inali yaikuru m'Samaria.
3 Ndipo Ahabu anaitana Obadiya woyang'anira nyumba yace. Koma Obadiya anaopa ndithu Yehova;
4 pakuti pamene Yezebeli anapulula aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri zana limodzi, nawabisa makumi asanu asanu m'phanga, nawadyetsa mkate ndi madzi.