1 Ndipo Solomo anapalana ubwenzi ndi Farao mfumu ya Aigupto, natenga mwana wamkazi wa Farao, nadza naye ku mudzi wa Davide, mpaka atamanga nyumba ya iye yekha, ndi nyumba ya Yehova, ndi linga lozinga Yerusalemu.
2 Koma anthu anaphera nsembe pamisanje, popeza panalibe nyumba yomangira dzina la Yehova kufikira masiku omwewo.
3 Ndipo Solomo anakondana ndi Yehova, nayenda m'malemba a Davide atate wace; koma anaphera nsembe nafukiza zonunkhira pamisanje.
4 Ndipo mfumu inapita ku Gibeoni kukaphera nsembe kumeneko; popeza msanje waukuru unali kumeneko, Solomo anapereka nsembe zopsereza cikwi cimodzi pa guwalo la nsembe.