1 Ndipo mfumu Solomo anali mfumu ya Israyeli yense.
2 Ndipo akuru a mfumu ndi awa: Azariya mwana wa Zadoki anali nduna,
3 Elihorepa ndi Ahiya ana a Sisa alembi, Yehosafati mwana wa Ahiludi wolembera mbiri,
4 ndi Benaya mwana wa Yehoyada anali kazembe wa nkhondo, ndi Zadoki ndi Abyatara anali ansembe,
5 ndi Azariya mwana wa Natani anayang'anira akapitao, ndi Zabudi mwana wa Natani anali nduna yopangira mfumu,
6 ndi Ahisara anayang'anira banja la mfumu, ndi Adoniramu mwana wa Abida anali wamsonkho.
7 Ndipo Solomo anali nao akapitao khumi ndi awiri akuyang'anira Aisrayeli onse, akufikitsira mfumu ndi banja lace zakudya; ali yense anafikitsa zakudya zofikira mwezi umodzi wa caka.