14 Abinadabu mwana wa Ido ku Nahanaimu;
15 Ahimazi ku Nafitali, iyeyu adakwatira Basemati mwana wa Solomo;
16 Baana mwana wa Husayi ku Aseri ndi ku Aloti;
17 Yehosafati mwana wa Paruwa ku Isakara;
18 Simeyi mwana wa Ela ku Benjamini;
19 Geberi mwana wa Uri ku dziko la Gileadi, dziko la Sihoni mfumu ya Aamori, ndi la Ogi mfumu ya Basani; munalibe kapitao wina m'deramo.
20 Ayuda ndi Aisrayeli anacuruka ngati mcenga wa kunyanja, namadya namamwa namakondwera.