8 Ndipo maina ao ndiwo: Benhuri anatengetsa ku mapiri a Efraimu;
9 Bendekeri ku Makazi ndi Saalibimu ndi Betsemesi ndi Elonibetanani;
10 Benhesedi ku Aruboti ndi Soko ndi dziko lonse la Heferi;
11 Benabinadabu ku mtunda wa Dori, mkazi wace ndiye Tafati mwana wa Solomo;
12 Baana mwana wa Ahiludi ku Tanaki ndi Megido ndi Betseani konse, ali pafupi ndi Zaratana kunsi kwa Yezreeli, kuyambira ku Betseani kufikira ku Abelimehola, kufikiranso kundunji ku Yokineamu;
13 Benigeheri ku Ramoti Gileadi, iyeyo anali nayo midzi ya Yairo mwana wa Manase iri m'Gileadiyo, iye anali nalo dziko la Arigobi liri m'Basani, midzi yaikuru makumi asanu ndi limodzi yamalinga ndi zitseko zamkuwa;
14 Abinadabu mwana wa Ido ku Nahanaimu;