4 Ndipo mlandu wa munthu wakupha mnzace wakuthawirako nakhala ndi moyo ndiwo: wakupha mnzace osati dala, osamuda kale lonse;
5 monga ngati munthu analowa kunkhalango ndi mnzace kutema mitengo, ndi dzanja lace liyendetsa nkhwangwa kutema mtengo, ndi nkhwangwa iguruka m'mpinimo, nikomana ndi mnzace, nafa nayo; athawire ku wina wa midzi iyi, kuti akhale ndi moyo;
6 kuti wolipsa mwazi angalondole wakupha mnzace, pokhala mtima wace watentha, nampeza, popeza njira njaitali, namkantha kuti wafa; angakhale sanaparamula imfa, poona sanamuda kale lonse.
7 Cifukwa cace ndikuuzani ndi kuti, Mudzipatulire midzi itatu.
8 Ndipo Yehova Mulungu wanu akakulitsa malire anu, monga analumbirira makolo anu, ndi kukupatsani dziko lonse limene ananena kwa makolo anu kuwapatsa ili;
9 ukadzasunga lamulo ili lonse kulicita, limene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m'njira zace masiku onse; pamenepo mudzionjezere midzi itatu yina pamodzi ndi itatu iyi;
10 kuti angakhetse mwazi wosacimwa pakati pa dziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu, pangakhale mwazi pa inu.