2 Ndipo Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,
3 Yakwanira nthawi yakupaza inu phiri ili; tembenukani kumka kumpoto,
4 Ndipo uuze anthu, ndi kuti, Mukapite kubzyola malire a abale anu, ana a Bsau okhala m'Seiri; ndipo adzakuopani; mucenjere ndithu;
5 musalimbana nao; popeza sindikupatsakoni dziko lao, pangakhale popondapo phazi lanu ai pakuti ndapatsa Bsau phiri la Seiri likhale lace lace.
6 Mugulane nao cakudya ndi ndarama, kuti mudye; mugulane naonso madzi kuti mumwe.
7 Pakuti Yehova Mulungu wanu anakudalitsani mu nchito zonse za manja anu; anadziwa kuyenda kwanu m'cipululu ici cacikuru; zaka izi makumi anai Yehova Mulungu wanu anakhala ndi inu; simunasowa kanthu.
8 Potero tinapitirira abale athu, ana a Bsau okhala m'Seiri, njira ya cidikha, ku Elati ndi ku Ezioni Geberi.