38 Imene inadya mafuta a nsembe zao zophera,Nimwa vinyo wa nsembe yao yothira?Iuke nikuthandizeni, Ikhale pobisalapo panu.
39 Tapenyani tsopano kuti Ine ndine iye,Ndipo palibe mulungu koma Ine;Ndipha Ine, ndikhalitsanso ndi mayo:Ndikantha, ndicizanso Ine;Ndipo palibe wakulanditsa m'dzanja langa.
40 Pakuti ndikweza dzanja langa kuloza kumwamba,Ndipo nditi, Pali moyo wanga kosatha,
41 Ndikanola lupanga langa lonyezimira,Ndi dzanja langa likagwira ciweruzo;Ndidzabwezera cilango ondiukira,Ndi kulanga ondida.
42 Mibvi yanga ndiiledzeretsa nao mwazi,Ndi lupanga langa lidzalusira nyama;Ndi mwazi wa ophedwa ndi ogwidwa,Ndi mutu wacitsitsi wa mdani,
43 Kondwerani, amitundu inu, ndi anthu ace;Adzalipsira mwazi wa atumiki ace,Adzabwezera cilango akumuukira,Nadzafafanizira zoipa dziko lace, ndi anthu ace.
44 Ndipo anadza Mose nanena mau onse a nyimbo iyi m'makutu mwa anthu, iye, ndi Hoseya mwana wa Nuni.