10 Koma ziti zonse ziribe zipsepse ndi mamba m'nyanja, ndi m'mitsinje, mwa zonse zokwawa za m'madzi, ndi mwa zamoyo zonse ziri m'madzi, muziziyesa zonyansa;
11 inde muziyese zonyansa; musamadya nyama zao; mitembo yao zikunyansireni.
12 Ziri zonse zopanda zipsepse kapena mamba m'madzimo muziyese zonyansa.
13 Ndipo mwa mbalame muziziyesa zonyansa izi; siziyenera kuzidya, zonyansa ndi izi: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi;
14 ndi muimba, ndi mphamba mwa mtundu wace;
15 kungubwi mwa mtundu wace;
16 ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi mwa mtundu wace;