14 ndi muimba, ndi mphamba mwa mtundu wace;
15 kungubwi mwa mtundu wace;
16 ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi mwa mtundu wace;
17 ndi nkhutunkhutu ndi nswankhono ndi mancici;
18 tsekwe, bvuwo, ndi dembu;
19 indwa, ndi cimeza monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.
20 Zokwawa zonse zakuuluka zokhala ndi miyendo inai, muziyesa izi zonyansa,