15 kungubwi mwa mtundu wace;
16 ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi mwa mtundu wace;
17 ndi nkhutunkhutu ndi nswankhono ndi mancici;
18 tsekwe, bvuwo, ndi dembu;
19 indwa, ndi cimeza monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.
20 Zokwawa zonse zakuuluka zokhala ndi miyendo inai, muziyesa izi zonyansa,
21 Koma muyenera kudya izi mwa zokwawa zonse zakuuluka, zokhala ndi miyendo inai, zokhala ndi miyendo pa mapazi ao, ya kuthumpha nayo pansi; mwa zimenezi muyenera kudya izi: