3 Nyama iri yonse yogawanika ciboda, nikhala yogawanikadi ciboda, ndi yobzikula, imeneyo muyenera kudya.
4 Koma izi zokha simuyenera kuzidya mwa zobzikulazo, kapena zogawanika ciboda; ngamila, angakhale abzikula, koma yosagawanika ciboda, muziiyesa yodetsedwa.
5 Ndi mbira, ingakhale ibzikula koma yosagawanika ciboda, muiyese yodetsedwa.
6 Ndi kalulu, popeza abzikula koma wosagawanika ciboda, mumuyese wodetsedwa.
7 Ndi nkhumba, popeza igawanika ciboda, nikhala yogawanikadi ciboda, koma yosabzikula, muiyese yodetsedwa.
8 Nyama yace musamaidya, mitembo yace musamaikhudza; muziyese zodetsedwa.
9 Mwa zonse ziri m'madzi muyenera kumadya izi: ziri zonse ziti nazo zipsepse ndi mamba m'madzi, m'nyanja, ndi m'mitsinje, zimenezo muyenera kumadya.