39 Ndipo ikafa nyama yakudya, iye amene akhudza mtembo wace adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
40 Ndipo iye wakudya kanthu ka mtembo wace azitsuka zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; iyenso wakunyamula mtembo wace atsuke zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
41 Ndipozokwawazonsezakukwawa pa dziko lapansi zikhale zonyansa; musamazidya.
42 Zonse zoyenda cafufumimba, ndi zonse za miyendo inai, kapena zonse zokhala nayo miyendo yambiri ndi zokwawa zonse zakukwawa pansi, musamazidya; popeza ndizo zonyansa.
43 Musamadzinyansitsa ndi cokwawa ciri conse cakukwawa, musamadzidetsa nazo, kuti mukadziipse nazo.
44 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu; potero dzipatuleni, ndipo muzikhala oyera; pakuti Ine ndine woyera; ndipo musamadziipsa ndi cokwawa ciri conse cakukwawa pansi.
45 Pakuti Ine ndine Yehova amene ndinakukwezani kukuturutsani m'dziko la Aigupto, ndikhale Mulungu wanu; cifukwa cace mukhale oyera, popeza ine ndine woyera.