9 Mwa zonse ziri m'madzi muyenera kumadya izi: ziri zonse ziti nazo zipsepse ndi mamba m'madzi, m'nyanja, ndi m'mitsinje, zimenezo muyenera kumadya.
10 Koma ziti zonse ziribe zipsepse ndi mamba m'nyanja, ndi m'mitsinje, mwa zonse zokwawa za m'madzi, ndi mwa zamoyo zonse ziri m'madzi, muziziyesa zonyansa;
11 inde muziyese zonyansa; musamadya nyama zao; mitembo yao zikunyansireni.
12 Ziri zonse zopanda zipsepse kapena mamba m'madzimo muziyese zonyansa.
13 Ndipo mwa mbalame muziziyesa zonyansa izi; siziyenera kuzidya, zonyansa ndi izi: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi;
14 ndi muimba, ndi mphamba mwa mtundu wace;
15 kungubwi mwa mtundu wace;