13 pamenepo wansembe aone, ndipo taonani, ngati khate lakuta thupi lace, amuche woyera wanthendayo; patuwa ponsepo; ndiye woyera.
14 Koma tsiku liri lonse ukaoneka pa iye mnofu wofiira, adzakhala wodetsedwa,
15 Ndipo wansembe aone mnofu wofiirawo, namuche wodetsedwa; mnofu wofiira ndiwo wodetsa; ndilo khate.
16 Kapena mnofu wofiira ukasandukanso, nusandulika wotuwa, afike kwa wansembe,
17 ndi wansembe amuone, ndipo taonani, ngati nthenda yasandulika yotuwa, wansembe amuche woyera wanthendayo; ndiye woyera.
18 Ndipo pamene thupi liri ndi cironda pakhungu pace, ndipo capola,
19 ndipo padali cironda pali cotupa coyera, kapena cikanga cotuuluka, pamenepo acionetse kwa wansembe; ndipo wansembe aone,